Apolisi mum’zinda wa Blantyre atsimikiza za imfa yabambo wina wazaka 46 yemwe wafa atagwera muchimbudzi chokumba.
M’neneri wa Polisi ya Limbe Patrick Mussa ndiye watsimikiza nkhani-yi ponena kuti ngozi-yi yachitikira kwa Kachere dzulo ndipo bamboyu dzina lake ndi Munana Mitambo.
A Mussa ati malemuwa adagwera muchimbudzi pomwe iwo amakoza denga la chimbudzi-chi kuti madzi amvula asamagwere mkati.
A Mussa apitiliza kunena kuti malemuwa anawatengera pachipatala cha Queen Elizatheth ndipo zotsatira zakuchipatala zaonetsa kuti malemuwa amwalira kaamba kovulala kwambiri m’mutu kutsatira ngozi yomwe inachitikayi.
Malinga ndi a Mussa a Mitambo anali ochokera m’mudzi mwa a Kachere mfumu yaikulu Machinjiri m’muzinda omwewu wa Blantyre.
AvantNewsFlash
Share this article